Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 12:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Uziturutsa akatundu ako usana pamaso pao, ngati a pa ulendo wa kundende; ndipo madzulo uzituruka wekha pamaso pao, monga amaturuka olowa kundende.

5. Udziboolere khoma pamaso pao, nuwaturutsire akatundu pamenepo,

6. Pamaso pao uwasenze paphewa pako, ndi kuwaturutsa kuli mdima, nuphimbe nkhope yako kuti usapenye dziko; popeza ndakuika cizindikilo ca nyumba ya Israyeli.

7. Ndipo ndinacita monga momwe anandilamulira, ndinaturutsa akatundu anga usana, ngati a pa ulendo wa kundende, ndi madzulo ndinaboola pakhoma ndi dzanja langa, ndinawaturutsa pali mdima, ndi kuwasenza paphewa panga pamaso: pao.

8. Ndipo m'mawa mau a Yehova anandidzera, ndi kuti,

9. Wobadwa ndi munthu iwe, kodi nyumba ya Israyeli, nyumba yampanduko, siinati kwa iwe. Ucitanji?

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 12