Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 12:16-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Koma ndidzawasiya owerengeka apulumuke lupanga, ndi njala, ndi mliri, kuti afotokoze zonyansa zao kwa amitundu kumene afikako; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

17. Anandidzeranso mau a Mulungu, akuti,

18. Wobadwa ndi munthu iwe, udye mkate wako ndi kunthunthumira, ndi kumwa madzi ako ndi kunjenjemera, ndi kutenga nkhawa;

19. nunene kwa anthu a m'dziko, Atero Yehova Mulungu za iwo okhala m'Yerusalemu, ndi za dziko la Israyeli, Adzadya mkate wao ndi nkhawa, ndi kumwa madzi ao ndi kusumwa; pakuti dziko lao lidzakhala lacipululu, kuleka kudzala kwace cifukwa ca ciwawa ca onse okhalamo.

20. Ndi midzi yokhalamo anthu idzapasuka, ndi dziko lidzakhala labwinja; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

21. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

22. Wobadwa ndi munthu iwe, ngwotani mwambi umene muli nao m'dziko la Israyeli, wakuti, Masiku acuruka, ndi masomphenya ali onse apita pacabe?

23. Cifukwa cace unene nao, Atero Yehova Mulungu, Ndidzaleketsa mwambi uwu, ndipo sadzauchulanso mwambi m'Israyeli; koma unene nao, Masiku ayandikira, nadzacitika masomphenya ali onse.

24. Pakuti sikudzakhalanso masomphenya acabe, kapena ula wosyasyalika m'nyumba ya Israyeli.

25. Pakuti Ine ndine Yehova, ndidzanena, ndi mau ndidzanenawo adzacitika, osazengerezekanso; pakuti m'masiku anu, nyumba yopanduka inu, ndidzanena mau ndi kuwacita, ati Yehova Mulungu.

26. Anandidzeranso mau a Yehova, akuti,

27. Wobadwa ndi munthu iwe, taona, iwo a nyumba ya Israyeli akuti, masomphenya awaona ndiwo a masiku ambiri: ndipo anenera za nthawi ziri kutali,

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 12