Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 4:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atamva tsono a adani Yuda ndi Benjamini kuti ana aja a ndende analikumangira Yehova Mulungu wa Israyeli Kacisi,

2. anayandikira kwa Zerubabele, ndi kwa akulu a nyumba za makolo, nanena nao, Timange pamodzi nanu; pakuti timfuna Mulungu wanu monga inu, ndipo timamphera nsembe ciyambire masiku a Ezaradoni mfumu ya Asuri, amene anatikweretsa kuno.

3. Koma Zerubabele, ndi Yesuwa, ndi akuru otsala a nyumba za makolo a Israyeli, anati kwa iwo, Sikuyenera ndi inu ndi ife kumangira Mulungu wathu nyumba, koma ife tokha pamodzi tidzamangira Yehova Mulungu wa Israyeli, monga mfumu Koresi mfumu ya Perisiya watilamulira.

4. Pamenepo anthu a m'dziko anafoketsa manja a anthu Ayuda, nawabvuta pomanga,

5. nalembera opangira atsutsane nao, nafafanize uphungu wao, masiku onse a Koresi mfumu ya Perisiya, mpaka ufumu wa Dariyo mfumu ya Perisiya.

6. Ndipo pokhala mfumu Ahaswero, poyambira ufumu wace, analembera cowaneneza okhala m'Yuda ndi m'Yerusalemu.

7. Ndipo masiku a Aritasasta Bisilamu, Mitiredati, Tabeeli, ndi anzao otsala, analembera kwa Aritasasta mfumu ya Perisiya; ndi cilembedwe cace ca kalatayo anamlemba m'Ciaramu, namsanduliza m'Ciaramu.

Werengani mutu wathunthu Ezara 4