Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 3:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Utakhala tsono mwezi wacisanu ndi ciwiri, ana a Israyeli ali m'midzimo, anthuwo anasonkhana ngati munthu mmodzi ku Yerusalemu.

2. Nanyamuka Yesuwa mwana wa Yozadaki, ndi abale ace ansembe, ndi Zerubabele mwana wa Sealitiyeli, ndi abale ace, namanga guwa la nsembe la Mulungu wa Israyeli, kuperekapo nsembe zopsereza, monga mulembedwa m'cilamulo ca Mose munthu wa Mulungu.

3. Ndipo anakhazika guwa la nsembe patsinde pace cifukwa ca kuopa iwo anthu a m'maikomo; nakwezera Yehova nsembe zopsereza pamenepo, nsembe zopsereza zam'mawa ndi zamadzulo.

Werengani mutu wathunthu Ezara 3