Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Estere 9:21-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. kuwalimbikitsira, asunge tsiku lakhumi ndi cinai, mwezi wa Adara, ndi tsiku lace lakhumi ndi cisanu lomwe, caka ndi caka,

22. ndiwo masiku amene Ayuda anapumula pa adani ao; ndi mwezi wacisoni unawasandulikira wakukondwera, ndi wamaliro ukhale tsiku lokoma, awayese masiku amadyerero ndi akukondwera, akutumizirana magawo, ndi akupatsa zaufulu kwa osauka.

23. Ndipo Ayuda anabvomereza kucita monga umo adayambira, ndi umo Moredekai adawalembera;

24. popeza Hamani mwana wa Hamedata wa ku Agagi, mdani wa Ayuda onse, adapangira Ayuda ciwembu kuwaononga, naombeza Puri, ndiwo ula, kuwatha ndi kuwaononga;

25. koma pofika mlanduwo kwa mfumu, anati mwa akalata kuti ciwembu cace coipa adacipangira Ayuda, cimbwerere mwini; ndi kuti Iye ndi ana amuna ace apacikidwe pamtengo,

26. Cifukwa cace anacha masikuwa Purimu, ndilo dzina la ulawo. Momwemo, cifukwa ca mau onse a kalatayo, ndi izi adaziona za mlanduwo, ndi ici cidawadzera,

27. Ayuda anakhazikitsa ici, nadzilonjezetsa okha, ndi mbeu yao, ndi onse akuphatikana nao, cingalekeke, kuti adzasunga masiku awa awiri monga mwalembedwa, ndi monga mwa nyengo yao yoikika, caka ndi caka;

28. ndi kuti masikuwa adzakumbukika ndi kusungika mwa mibadwo yonse, banja liri lonse, dziko liri lonse, ndi mudzi uli wonse; ndi kuti masiku awa sadzalekeka mwa Ayuda, kapena kusiyidwa cikumbukilo cao mwa mbeu yao.

29. Pamenepo Estere mkazi wamkuru mwana wa Abihaili, ndi Moredekai Myuda, analembera molamulira, kukhazikitsa kalata uyu waciwiri wa Purimu.

30. Natumiza iye akalata kwa Ayuda onse, ku maiko zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi awiri a ufumu wa Ahaswero, ndiwo mau a mtendere ndi coonadi;

Werengani mutu wathunthu Estere 9