Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Estere 3:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo Hamani anati kwa mfumu Ahaswero, Pali mtundu wina wa anthu obalalika ndi ogawanikana mwa mitundu ya anthu m'maiko onse a ufumu wanu, ndi malamulo ao asiyana nao a anthu onse, ndipo sasunga malamulo a mfumu; cifukwa cace mfumu siiyenera kuwaleka.

9. Cikakomera mfumu, cilembedwe kuti aonongeke iwo; ndipo ndidzapereka matalente a siliva zikwi khumi m'manja a iwo akusunga nchito ya mfumu, abwere nao kuwaika m'nyumba za cuma ca mfumu.

10. Ndipo mfumu inabvula mphete yace pa cala cace, naipereka kwa Hamani mwana wa Hamedata wa ku Agagi, mdani wa Ayuda.

11. Ndipo mfumu idati kwa Hamani, Siliva akhale wako, ndi anthu omwe; ucite nao monga momwe cikukomera.

12. Pamenepo anaitana alembi a mfumu mwezi woyamba, tsiku lace lakhumi ndi citatu, nalembera monga mwa zonse Hamani analamulira akazembe ndi ziwanga zoyang'anira maiko ali onse, ndi akalonga a mitundu iri yonse ya anthu, maiko ali onse monga mwa cilembedwe cao, ndi mitundu iri yonse ya anthu monga mwa cinenedwe cao; anazilemba m'dzina la mfumu Ahaswero, nazisindikiza ndi mphete ya mfumu.

13. Ndipo anatumiza akalata ndi amtokoma ku maiko onse a mfumu, kuti aononge, aphe, napulule Ayuda onse, ndiwo ana, ndi okalamba, makanda, ndi akazi, tsiku limodzi, ndilo tsiku lakhumi ndi citatu la mwezi wakhumi ndi ciwiri, ndiwo mwezi wa Adara; nalande zao mofunkha.

14. Mau a colembedwaco, ndiwo kuti licitike lamulo m'maiko onse, analalikidwa kwa anthu onse, kuti akonzekeretu tsiku lomwelo.

Werengani mutu wathunthu Estere 3