Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 8:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo acule adzakwera pa iwe, ndi pa anthu ako, ndi pa anyamata ako onse.

5. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Nena ndi Aroni, Tambasula dzanja lako ndi ndodo yako, panyanja, pangalande, ndi pamatamanda, nukweretse acule pa dziko la Aigupto.

6. Ndipo Aroni anatambasula dzanja lace pa madzi a m'Aigupto; ndipo anakwera acule, nakuta dziko la Aigupto.

7. Ndipo alembi anacita momwemo ndi matsenga ao, nakweretsa acule pa dziko la Aigupto.

8. Pamenepo Farao anaitana Mose ndi Aroni, nati, Mundipembere Yehova, kuti andicotsere ine ndi anthu anga aculewo; ndipo ndidzalola anthu amuke, kuti amphere Yehova nsembe.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 8