Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 5:6-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo tsiku lomwelo Farao analamulira akufulumiza anthu, ndi akapitao ao, ndi kuti,

7. Musawapatsanso anthu udzu wakupanga nao njerwa monga kale; apite okha adzifunire udzu.

8. Ndipo muziwawerengera njerwa, monga momwe anapanga kale; musacepsapo, popeza acita cilezi; cifukwa cace alikupfuula, ndi kuti, Timuke, timphere nsembe Mulungu wathu.

9. Ilimbike nchito pa amunawo, kuti aigwiritsitse, asasamalire mau amabodza.

10. Ndipo akufulumiza anthu ndi akapitao ao anaturuka, nanena ndi anthu ndi kuti, Atero Farao, Kulibe kukupatsani udzu.

11. Mukani inu nokha, dzifunireni udzu komwe muupeza; pakuti palibe kanthu kadzacepa pa nchito yanu.

12. Pamenepo anthuwo anabalalika m'dziko lonse la Aigupto kufuna ciputu ngati udzu.

13. Ndipo akufulumiza anawakakamiza, ndi kuti, Tsirizani nchito zanu, nchito ya tsiku pa tsiku lace, monga muja munali ndi udzu.

14. Ndipo anapanda akapitao a ana a Israyeli, amene ofulumiza a Farao adawaika, ndi kuti, Nanga dzulo ndi lero simunatsiriza bwanji nchito yanu yoneneka ya njerwa, monga kale?

15. Pamenepo akapitao a ana a Israyeli anafika nalirira Farao, nati, Mwatero bwanji ndi akapolo anu?

16. Udzu osawapatsa akapolo anu, ndipo amanena ndi ife, Umbani njerwa; ndipo, taonani, amapanda akapolo anu; koma kulakwa nkwa anthu anu.

17. Koma iye anati, Aulesi inu, aulesi: cifukwa cace mulikunena, Timuke, timphere nsembe Yehova.

18. Mukani tsopano, gwirani nchito; pakuti sadzakupatsani udzu, koma muonetse ciwerengero cace ca njerwa.

19. Ndipo akapitao a ana a Israyeli anaona kuti kudawaipira, pamene ananena, Musamacepetsa njerwa zanu, nchito ya tsiku pa tsiku lace.

20. Ndipo poturuka kwa Farao iwo anakomana ndi Mose ndi Aroni, alikuima popenyana nao;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 5