Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 5:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. ndipo ananena nao, Yehova akupenyeni, naweruze; pakuti mwatinyansitsa pamaso pa Farao, ndi pamaso pa anyamata ace, ndi kuwapatsa lupanga m'dzanja lao kutipha nalo.

22. Pamenepo Mose anabwerera namka kwa Yehova, nati, Ambuye, mwawacitiranji coipa anthuwa? mwandituma bwanji?

23. Popeza kuyambira kuja ndinafika kwa Farao kulankhula m'dzina lanu, anawacitira coipa anthuwa; ndipo simunalanditsa anthu anu konse.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 5