Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 5:11-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Mukani inu nokha, dzifunireni udzu komwe muupeza; pakuti palibe kanthu kadzacepa pa nchito yanu.

12. Pamenepo anthuwo anabalalika m'dziko lonse la Aigupto kufuna ciputu ngati udzu.

13. Ndipo akufulumiza anawakakamiza, ndi kuti, Tsirizani nchito zanu, nchito ya tsiku pa tsiku lace, monga muja munali ndi udzu.

14. Ndipo anapanda akapitao a ana a Israyeli, amene ofulumiza a Farao adawaika, ndi kuti, Nanga dzulo ndi lero simunatsiriza bwanji nchito yanu yoneneka ya njerwa, monga kale?

15. Pamenepo akapitao a ana a Israyeli anafika nalirira Farao, nati, Mwatero bwanji ndi akapolo anu?

16. Udzu osawapatsa akapolo anu, ndipo amanena ndi ife, Umbani njerwa; ndipo, taonani, amapanda akapolo anu; koma kulakwa nkwa anthu anu.

17. Koma iye anati, Aulesi inu, aulesi: cifukwa cace mulikunena, Timuke, timphere nsembe Yehova.

18. Mukani tsopano, gwirani nchito; pakuti sadzakupatsani udzu, koma muonetse ciwerengero cace ca njerwa.

19. Ndipo akapitao a ana a Israyeli anaona kuti kudawaipira, pamene ananena, Musamacepetsa njerwa zanu, nchito ya tsiku pa tsiku lace.

20. Ndipo poturuka kwa Farao iwo anakomana ndi Mose ndi Aroni, alikuima popenyana nao;

21. ndipo ananena nao, Yehova akupenyeni, naweruze; pakuti mwatinyansitsa pamaso pa Farao, ndi pamaso pa anyamata ace, ndi kuwapatsa lupanga m'dzanja lao kutipha nalo.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 5