Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 4:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. kuti akhulupirire kuti wakuonekera Yehova Mulungu wa makolo ao, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.

6. Ndipo Yehova ananenanso naye, Longa dzanja lako pacifuwa pako. Ndipo analonga dzanja lace pacifuwa pace, naliturutsa, taonani, dzanja lace linali lakhate, lotuwa ngati cipale cofewa.

7. Ndipo ananena iye, Bwerezanso dzanja lako pacifuwa pako. Ndipo anabwerezanso dzanja lace pacifuwa pace; naliturutsa pacifuwa pace, taonani, linasandukanso lomwe lakale.

8. Ndipo kudzatero, ngati sakhulupirira iwe, ndi kusamvera mau a cizindikilo coyamba, adzakhulupirira mau a cizindikilo cotsirizaci.

9. Ndipo kudzatero, aka panda kukhulupirira zingakhale zizindikilo izi, ndi kusamvera mau ako, ukatunge madzi a kunyanja, ndi kuthira pamtunda; ndi madzi watunga ku nyanjayo adzasanduka mwazi pamtunda.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 4