Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 39:34-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. ndi cophimba ca zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiirira, ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi nsaru yocinga yotsekera;

35. likasa la mboni, ndi mphiko zace, ndi cotetezerapo;

36. gomelo, zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;

37. coikapo nyali coona, nyali zace, ndizo nyali zimakonzekazi, ndi zipangizo zace zonse, ndi mafuta a kuunikira;

38. ndi guwa la nsembe lagolidi, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pa khomo la cihemaco;

39. guwa la nsembe lamkuwa, ndi made ace amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;

40. nsaru zocingira za pabwalo, osici zace, ndi makamwa ace, ndi nsaru yotsekera pa cipata ca pabwalo, zingwe zace, ndi ziciri zace, ndi zipangizo zonse za nchito ya kacisi, za ku cihema cokomanako;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 39