Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 39:30-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ndipo anapanga phanthiphanthi wa korona wopatulika wa golidi woona, nalembapo lemba, ngati malocedwe a cosindikizira, KUPATULIKIRA YEHOVA.

31. Namangako mkuzi wamadzi, kuumanga nao pamwamba pa nduwira; monga Yehova adamuuza Mose.

32. Potero anatsiriza nchito yonseya kacisi wa cihema cokomanako; ndipo ana a Israyeli adacita monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, anacita momwemo.

33. Ndipo anabwera naye kacisi kwa Mose, cihemaco, ndi zipangizo zace zonse, zokowera zace, matabwa ace, mitanda yace, ndi mizati yace, nsanamira zace ndi nsici zace, ndi makamwa ace;

34. ndi cophimba ca zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiirira, ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi nsaru yocinga yotsekera;

35. likasa la mboni, ndi mphiko zace, ndi cotetezerapo;

36. gomelo, zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;

37. coikapo nyali coona, nyali zace, ndizo nyali zimakonzekazi, ndi zipangizo zace zonse, ndi mafuta a kuunikira;

38. ndi guwa la nsembe lagolidi, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pa khomo la cihemaco;

39. guwa la nsembe lamkuwa, ndi made ace amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 39