Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 39:16-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Anapanganso zoikamo ziwiri zagolidi, ndi mphete ziwiri zagolidi; naika mphete ziwirizo pa nsonga ziwiri za capacifuwa.

17. Ndipo anamanga maunyolo awiri opota agolidi pa mphete ziwiri pa nsonga za capacifuwa.

18. Ndi nsonga zace ziwiri zina za maunyolo awiri opotawo anazimanga pa zoikamo ziwiri, nazimanga pa zapamapewa za efodi, m'tsogolo mwace.

19. Ndipo anapanga mphete ziwiri zagolidi, naziika pa nsonga ziwiri za capacifuwa, m'mphepete mwace m'katimo, pa mbali ya kuefodi.

20. Ndipo anapanga mphete ziwiri zagolidi, naziika pa zapamapewa ziwiri za efodi pansi pace, pa mbali yace ya kutsogolo, pafupi pa msoko wace, pamwamba pa mpango wa efodi.

21. Ndipo anamanga capacifuwa pa mphete zace ndi mphete za efodi ndi mkuzi wamadzi, kuti cikhale pa mpango wa efodi, ndi kuti capacifuwa cisamasuke paefodi; monga Yehova anamuuza Mose.

22. Ndipo anaomba mwinjiro wa efodi, nchito yoomba ya lamadzi lokha;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 39