Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 38:8-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo anapanga mkhate wamkuwa, ndi tsinde lace lamkuwa, wa akalirole a akazi otumikira, akutumikira pa khomo la cihema cokomanako.

9. Ndipo anapanga bwalo; pa mbali ya kumwela, kumwela, nsaru zocingira za pabwalo zinali za bafuta wa thonje losansitsa, mikono zana limodzi;

10. nsici zace makumi awiri, ndi makamwa ao makumi awiri, amkuwa; zokowera za nsici ndi mitanda yace zasiliva.

11. Ndi pa mbali ya kumpoto mikono zana limodzi, nsici zace makumi awiri, nw makamwa ace makumi awiri, amkuwa; zokowera za nsici ndi mitanda yace yasiliva.

12. Ndi pa mbali ya kumadzulo panali nsaru zocingira za mikono makumi asanu, nsid zace khumi, ndi makamwa ace khumi; zokowera za nsici ndi mitanda yace yasiliva.

13. Ndi pa mbali ya kum'mawa, kum'mawa, mikono makumi asanu.

14. Nsaru zocingira za pa mbali imodzi ya cipata nza mikono khumi ndi isanu; nsici zace zitatu, ndi makamwa ace atatu;

15. momwemonso pa mbali yina: pa mbali yino ndi pa mbali yina ya cipata ca pabwalo panali nsaru zocingira za mikono khumi ndi isanu; nsici zace zitatu, ndi makamwa ace atatu.

16. Nsaru zocingira zonse za pabwalo pozungulira zinali za bafuta wa thonje losansitsa.

17. Ndipo makamwa a nsici anali amkuwa; zokowera za nsici ndi mitanda Iyace zasiliva; ndi zokutira mitu yace zasiliva; ndi nsici zonse za pabwalo zinagwirana pamodzi ndi siliva.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 38