Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 35:6-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. golidi, ndi siliva, ndi mkuwa; ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;

7. ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;

8. ndi mafuta akuunikira, ndi zonunkhira za mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma;

9. ndi miyala yasohamu, ndi miyala yoika ya efodi, ndi ya capacifuwa.

10. Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova anauza;

11. kacisi, hema wace, ndi cophimba cace, zokowera zace, ndi matabwa ace, mitanda yace, mizati, nsanamira, ndi nsici zace, ndi makamwa ao;

12. likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;

13. gome, ndi mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;

14. ndi coikapo nyali ca kuunika, ndi zipangizo zace, ndi nyali zace, ndi mafuta a kuunika;

15. ndi guwa la nsembe lofukizapo, ndi mphiko zace, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pakhomo, pa khomo la kacisi;

16. guwa la nsembe yopereza, ndi made amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;

17. nsaru zocingira za kubwalo, nsici zace, ndi makamwa ace, ndi nsaru yotsekera ku cipata ca pabwalo;

18. ziciri za cihema, ndi ziciri za kubwalo, ndi zingwe zao;

19. zobvala za kutumikira nazo m'maopatulika, zobvala zopatulika za. Aroni wansembe, ndi zobvala za ana ace, zakugwira nazo nchito ya nsembe.

20. Ndipo khamu lonse la ana a Israyeli linacoka pamaso pa Mose.

21. Ndipo anadza, ali yense wofulumidwa mtima, ndi yense mzimu wace wamfunitsa, nabwera naco copereka ca Yehova, ca ku nchito ya cihema cokomanako, ndi ku utumiki wace wonse, ndi ku zobvala zopatulika.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 35