Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 35:30-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ndipo Mose anati kwa ana a Israyeli, Taonani, Yehova anaitana, ndi kumchula dzina lace, Bezaleli, mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa pfuko la Yuda;

31. ndipo anamdzaza ndi mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi cidziwitso, za m'nchito ziri zonse;

32. kulingirira nchito zaluso, kucita ndi golidi, ndi siliva, ndi mkuwa;

33. ndi kuzokota miyala voikika, ndi kuzokota mitengo, kucita m'nchito ziri zonse zaluso.

34. Ndipo anaika m'mtima mwace kuti alangize ena, iye ndi Aholiabu mwana wa Ahisama, wa pfuko la Dani.

35. Amenewo anawadzaza ndi luso lamtima, lakucita nchito ziri zonse, ya kuzokota miyala, ndi ya mmisiri waluso, ndi ya wopikula ndi lamadzi ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ya muomba, ya iwo akucita nchito iri yonse, ndi ya iwo olingirira nchito yaluso.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 35