Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 32:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma pamene anaona kuti Mose anacedwa kutsika m'phiri, anthuwo anasonkhana kwa Aroni, nanena naye, Ukani, tipangireni milungu yakutitsogolera; pakuti Mose uyu, munthuyu anatikweza kucokera m'dziko la Aigupto, sitidziwa comwe camgwera.

2. Ndipo Aroni ananena nao, Thyolani mphete zagolidi ziri; m'makutu a akazi anu, a ana anu amuna ndi akazi, ndi kubwera nazo kwa ine.

3. Ndipo anthu onse anathyola mphete zagolidi zinali m'makutu mwao, nabwera nazo kwa Aroni.

4. Ndipo anazilandira ku manja ao, nacikonza ndi cozokotera, naciyenga mwana wa ng'ombe; ndipo anati, Siyi milungu yako, Israyeli, imene inakukweza kucokera m'dziko la Aigupto.

5. Pakuciona Aroni, anamanga guwa la nsembe patsogolo pace; ndipo Aroni anapfuula nati, Mawa aliko madyerero a Yehova.

6. Ndipo m'mawa mwace anauka mamawa, nafukiza nsembe zopsereza, nabwera nazo nsembe zamtendere; ndi anthu anakhala pansi kudya ndi kumwa, nauka kusewera.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 32