43. Ndipo pamenepo ndidzakomana ndi ana a Israyeli; ndipo cihema cidzapatulidwa ndi ulemerero wanga.
44. Ndipo ndidzapatula cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe; ndidzapatulanso Aroni ndi ana ace amuna omwe, andicitire nchito ya nsembe.
45. Ndipo ndidzakhala pakati pa ana a Israyeli, ndi kukhala Mulungu wao.
46. Ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wao, amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto, kuti ndikhale pakati pao. Ine ndine Yehova Mulungu wao.