Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 26:29-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndipo uzikuta matabwa ndi golidi, ndi kupanga mphete zao zagolidi zopisamo mitandayo; uzikutanso mitandayo ndi golidi.

30. Ndipo uutse kacisi monga mwa makhalidwe ace amene anakusonyeza m'phiri.

31. Ndipo uziomba nsaru yocinga ya thonje lamadzi, ndi lofiirira ndi lofiira, ndi la bafuta wa thonje losansitsa, aiombe ndi akerubi nchito ya mmisiri;

32. ndipo uicinge pa mizati inai ya mitengo wasitimu, zokuta ndi golidi; zokowera zao zikhale zagolidi, ndi makamwa anai asiliva.

33. Ndipo uzicinga nsaru yocinga pa zokowerazo, nulowetse likasa la mboni kukati kwa nsaru yocinga; ndipo nsaru yocingayo idzakugawirani pakati pa malo opatulika ndi malo opatulikitsa.

34. Ndipo uziika cotetezerapo pa likasa la mboni, m'malo opatulikitsa.

35. Nuziika gomelo kunja kwa nsaru yocinga, ndi coikapo nyali pandunji pa gome, pa mbali ya kumwela ya kacisi; koma uike gomelo pa mbali ya kumpoto,

36. Ndipo uziomba nsaru yotsekera pa khomo la bema, ya lakuda, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, nchito ya wopikula.

37. Ndipo uzipangira nsaru yotsekerayo nsanamira zisanu za mtengo wasitimu, ndi kuzikuta ndi golidi; zokowera zao zikhale zagolidi; nuziyengera makamwa asanu amkuwa.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 26