Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 23:16-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. ndi madyerero a masika, zipatso zoyamba za nchito zako, zimene udazibzala m'munda; ndi madyerero a kututa, pakutha caka, pamene ututa nchito zako za m'munda.

17. Katatu m'caka amuna onse azioneka pamaso pa Ambuye Yehova.

18. Usapereka mwazi wa nsembe yanga pamodzi ndi mkate wacotupitsa; ndi mafuta a madyerero anga asagonamo kufikira m'mawa.

19. Uzibweca nazo zoyambayamba za m'munda mwako ku nyumba ya Yehova Mulungu wako. Usaphike mwana wa mbuzi mu mkaka wa mace.Mulungu aloniezana nao za Kanani.

20. Taona, ndituma mthenga akutsogolere, kukusunga panjira, ndi kukufikitsa pamalo pomwe ndakonzeratu.

21. Musamalire iye, ndi kumvera mau ace; musamwawitsa mtima, pakuti sadzakhululukira zoo lakwa zanu; popeza dzina langa liri m'mtima mwace.

22. Pakuti ukamveratu mau ace, ndi kucita zonse ndizilankhula, ndidzakhala mdani wa adani ako, ndipo ndidzasautsa akusautsa iwe.

23. Pakuti mthenga wanga adzakutsogolera, nadzakufikitsa kwa Aamori, ndi Ahiti, ndi Aperizi, ndi Akanani, Ahivi, ndi Ayebusi; ndipo ndidzawaononga.

24. Usagwadira milungu yao, kapena kuwatumikira, kapena kucita monga mwa nchito zao; koma uwapasule konse, ndi kugamulatu zoimiritsa zao.

25. Ndipo muzitumikira Yehova Mulungu wanu, potero adzadalitsa cakudya cako, ndi madzi ako; ndipo ndidzacotsa nthenda pakati pa iwe.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 23