Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 21:21-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Koma akakhala wosafa tsiku limodzi kapena awiri, asalirike, pakuti ndiye ndalama ya mbuye wace.

22. Akayambana amuna, nakakantha mkazi ali ndi pakati, kotero kuti abala, koma alibe kuphwetekwa; alipe ndithu, monga momwe amchulira mwamuna wa mkaziyo; apereke monga anena oweruza.

23. Koma ngati kuphweteka kukalipo, uzipereka moyo kulipa moyo,

24. diso kulipa diso, dzino kulipa dzino, dzanja kulipa dzanja, phazi kulipa phazi,

25. kutentha kulipa kutentha, bala kulipa bala, mkwapulo kulipa mkwapulo.

26. Munthu akampanda mnyamata wace, kapena mdzakazi wace, padiso, nalithudzula, azimlola amuke waufulu cifukwa ca diso lace.

27. Ndipo akagurula dzino la mnyamata wace, kapena dzino la mdzakazi wace, azimlola amuke waufulu cifukwa ca dzino lace.

28. Ng'ombe ikatunga mwamuna kapena mkazi, nafa, aiponyetu miyala ng'ombeyo, osadya nyama yace; koma mwini ng'ombeyo azimasuka.

29. Koma ngati ng'ombe ikatunga masiku adapitawo, ndipo anamcenjeza mwiniyo, koma osaisunga iye, ndipo ikapha mwamuna kapena mkazi, aiponye miyala ng'ombeyo, ndi mwini waceyo amuphenso.

30. Akamuikira dipo, azipereka ciombolo ca moyo wace monga mwa zonse adamuikira.

31. Ingakhale yatunga mwana wamwamuna kapena wamkazi, aicitire monga mwa ciweruzo ici.

32. Ng'ombeyo ikatunga mnyamata kapena mdzakazi, azipatsa mbuye wace ndalama za masekele a siliva makumi atatu, ndipo ng'ombeyo aiponye miyala.

33. Munthu akafukula dzenje, kapena akakumba dzenje, osalibvundikira, ndipo ikagwamo ng'ombe kapena buru,

Werengani mutu wathunthu Eksodo 21