Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 21:14-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma munthu akacita dala pa mnzace, kumupha monyenga; uzimcotsa ku guwa langa la nsembe, kuti afe.

15. Munthuwakukanthaatatewace, kapena amai wace, aphedwe ndithu.

16. Iye wakuba munthu, angakhale wamgulitsa, kapena akampeza m'dzanja lace, aphedwe ndithu.

17. Munthu wakutemberera atate wace, kapena amai wace, aphedwe ndithu.

18. Akalimbana amuna, ndipo wina akakantha mnzace ndi mwala, kapena ndi nkhonyo, wosafa iye, koma wakhulungira pakama;

19. akaukanso, nakayendayenda pabwalo ndi ndodo yace, womkanthayo azikhala womasuka; pakutsotsa pace pokha azimbwezera, namcizitse konse.

20. Munthu akakantha mnyamata wace, kapena mdzakazi wace, ndi ndodo, ndipo akafa padzanja pace; ameneyo aliridwe ndithu.

21. Koma akakhala wosafa tsiku limodzi kapena awiri, asalirike, pakuti ndiye ndalama ya mbuye wace.

22. Akayambana amuna, nakakantha mkazi ali ndi pakati, kotero kuti abala, koma alibe kuphwetekwa; alipe ndithu, monga momwe amchulira mwamuna wa mkaziyo; apereke monga anena oweruza.

23. Koma ngati kuphweteka kukalipo, uzipereka moyo kulipa moyo,

24. diso kulipa diso, dzino kulipa dzino, dzanja kulipa dzanja, phazi kulipa phazi,

25. kutentha kulipa kutentha, bala kulipa bala, mkwapulo kulipa mkwapulo.

26. Munthu akampanda mnyamata wace, kapena mdzakazi wace, padiso, nalithudzula, azimlola amuke waufulu cifukwa ca diso lace.

27. Ndipo akagurula dzino la mnyamata wace, kapena dzino la mdzakazi wace, azimlola amuke waufulu cifukwa ca dzino lace.

28. Ng'ombe ikatunga mwamuna kapena mkazi, nafa, aiponyetu miyala ng'ombeyo, osadya nyama yace; koma mwini ng'ombeyo azimasuka.

29. Koma ngati ng'ombe ikatunga masiku adapitawo, ndipo anamcenjeza mwiniyo, koma osaisunga iye, ndipo ikapha mwamuna kapena mkazi, aiponye miyala ng'ombeyo, ndi mwini waceyo amuphenso.

30. Akamuikira dipo, azipereka ciombolo ca moyo wace monga mwa zonse adamuikira.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 21