9. Ndipo Yetero anakondwera cifukwa ca zabwino zonse Yehova adazicitira Israyeli, ndi kuwalanditsa m'dzanja la Aaigupto.
10. Nati Yetero, Woyamikika Yehova, amene anakulanditsani m'dzanja la Aaigupto, ndi m'dzanja la Farao; ameneanalanditsa anthu awa pansi pa dzanja la Aaigupto.
11. Tsopano ndidziwa kuti Yehova ali wamkuru ndi milungu yonse; pakuti momwe anadzikuza okha momwemo anawaposa,
12. Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose, anamtengera Mulungu nsembe Yopsereza, ndi nsembe zophera; ndipo Aroni ndi akuru onse a Israyeli anadza kudzadya mkate ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.
13. Ndipo kunatero kuti m'mawa mwace Mose anakhala pansi kuweruzira anthu mirandu yao; ndipo anthu anakhala ciriri pamaso pa Mose kuyambira m'mawa kufikira madzulo.