Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 18:19-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Tamvera mau anga tsopano, ndikupangire nzeru, ndi Mulungu akhale nawe; ukhale m'malo mwa anthu kwa Mulungu, nupite nayo mirandu kwa Mulungu;

20. nuwamasulire malemba, ndi malamulo, ndi kuwadziwitsa njira imene ayenera kuyendamo, ndi nchito imene ayenera kucita.

21. Koma iwe, dzisankhire mwa anthu ako onse, amuna amtima, akuopa Mulungu, amuna oona, akudana nalo phindu la cinyengo; nuwaikire iwo oterewa, akuru a pa zikwi, akuru a pa mazana, akuru a pa makumi asanu, akuru a pa makumi;

22. ndipo iwo aweruze mirandu ya anthu nthawi zonse; ndipo kudzakhala kuti mirandu yaikuru yonse abwere nayo kwa iwe; koma mirandu yaing'ono yonse aweruze okha; potero idzakucepera nchito, ndi iwo adzasenza nawe.

23. Ukacite cinthuci, ndi Mulungu akakuuza cotero, udzakhoza kupirira, ndi anthu awa onse adzapita kwao mumtendere.

24. Ndipo Mose anamvera mau a mpongozi wace, nacita zonse adazinena.

25. Ndipo Mose anasankha amuna amtima mwa Aisrayeli onse, nawaika akuru a pa anthu, akuru a pa zikwi, akuru a pa mazana, akuru a pa makumi asanu, ndi akuru a pa makumi.

26. Ndipo anaweruza anthu nthawi zonse; mlandu wakuwalaka amabwera nao kwa Mose, ndi milandu yaing'ono yonse amaweruza okha.

27. Ndipo Mose analola mpongozi wace amuke; ndipo anacoka kumka ku dziko lace.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 18