Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 18:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Udzalema konse, iwe ndi anthu amene uli nao; pakuti cikulaka cinthu ici; sungathe kucicita pa wekha.

19. Tamvera mau anga tsopano, ndikupangire nzeru, ndi Mulungu akhale nawe; ukhale m'malo mwa anthu kwa Mulungu, nupite nayo mirandu kwa Mulungu;

20. nuwamasulire malemba, ndi malamulo, ndi kuwadziwitsa njira imene ayenera kuyendamo, ndi nchito imene ayenera kucita.

21. Koma iwe, dzisankhire mwa anthu ako onse, amuna amtima, akuopa Mulungu, amuna oona, akudana nalo phindu la cinyengo; nuwaikire iwo oterewa, akuru a pa zikwi, akuru a pa mazana, akuru a pa makumi asanu, akuru a pa makumi;

22. ndipo iwo aweruze mirandu ya anthu nthawi zonse; ndipo kudzakhala kuti mirandu yaikuru yonse abwere nayo kwa iwe; koma mirandu yaing'ono yonse aweruze okha; potero idzakucepera nchito, ndi iwo adzasenza nawe.

23. Ukacite cinthuci, ndi Mulungu akakuuza cotero, udzakhoza kupirira, ndi anthu awa onse adzapita kwao mumtendere.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 18