Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 15:26-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. ndipo anati, Ngati udzamveratu mau a Yehova, Mulungu wako, ndi kucita zoona pamaso pace, ndi kuchera khutu pa malamulo ace, ndi kusunga malemba ace onse, za nthenda zonse ndinaziika pa Aaigupto sindidzaziika pa iwe nnena imodzi; pakuti Ine Yehova ndine wakuciritsa iwe.

27. Ndipo anafika pa Elimu, ndi pamenepo panali akasupe a madzi khumi ndi awiri, ndi akanjedza makumi asanu ndi awiri; ndipo anamanga cigono cao pomwepo pa madziwo.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 15