22. Ndipo Mose anatsogolera Israyeli kucokera ku Nyanja Yofiira, ndipo anaturukako nalowa m'cipululu ca Suri; nayenda m'cipululu masiku atatu, osapeza madzi.
23. Pamene anafika ku Mara, sanakhoza kumwa madzi a Mara, pakuti anali owawa; cifukwa cace anacha dzina lace Mara.
24. Ndipo anthu anadandaulira Mose, ndi kuti, Tidzamwa ciani?
25. Ndipo iye anapfuulira kwa Yehova; ndipo Yehova anamsonyeza mtengo ndipo anauponya m'madzimo, ndi madzi anasanduka okoma. Pamenepo anawapangira lemba ndi ciweruzo, ndi pomwepa anawayesa;