Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 15:19-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Pakuti akavalo a Farao analowa m'nyanja, ndi magareta ace ndi apakavalo ace, ndipo Yehova anawabwezera madzi a m'nyanja; koma ana a Israyeli anayenda pouma pakati pa nyanja.

20. Ndipo Miriamu mneneriyo, mlongo wa Aroni, anagwira lingaka m'dzanja lace; ndipo akazi onse anaturuka kumtsata ndi malingaka ndi kuthira mang'ombe.

21. Ndipo Miriamu anawayankha,Yimbirani Yehova, pakuti wapambanatu;Kavalo ndi wokwera wace anawaponya m'nyanja.Madzi a ku Mara.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 15