29. Koma ana a Israyeli anayenda pouma pakati pa nyanja; ndi madziwo anakhala ngati khoma kwa iwo, palamanja ndi palamanzere.
30. Comweco Yehova anapulumutsa Israyeli tsiku lomwelo m'manja a Aaigupto; ndipo Israyeli anaona Aaigupto akufa m'mphepete mwa nyanja.
31. Ndipo Israyeli anaiona nchito yaikuru imene Yehova anacitira Aaigupto, ndipo anthuwo anaopa Yehova; nakhulupirira Yehova ndi mtumiki wace Mose.