Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 14:29-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Koma ana a Israyeli anayenda pouma pakati pa nyanja; ndi madziwo anakhala ngati khoma kwa iwo, palamanja ndi palamanzere.

30. Comweco Yehova anapulumutsa Israyeli tsiku lomwelo m'manja a Aaigupto; ndipo Israyeli anaona Aaigupto akufa m'mphepete mwa nyanja.

31. Ndipo Israyeli anaiona nchito yaikuru imene Yehova anacitira Aaigupto, ndipo anthuwo anaopa Yehova; nakhulupirira Yehova ndi mtumiki wace Mose.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 14