Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 14:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Yehova adzakugwirirani nkhondo, ndipo inu mudzakhala cere.

15. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Upfuuliranji kwa Ine? lankhula ndi ana a Israyeli kuti aziyenda.

16. Ndipo iwe nyamula ndodo yako, nutambasulire dzanja lako kunyanja, nuigawe, kuti ana a Israyeli alowe pakati pa nyanja pouma.

17. Ndipo Ine, taonani, ndilimbitsa mitima ya Aaigupto, kuti alowemo powatsata; ndipo ndidzalemekezedwa pa Farao, ndi pa nkhondo yace yonse, pa magareta ace, ndi pa okwera pa akavalo ace.

18. Ndipo Aaigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, polemekezedwa Ine pa Farao, pa magareta ace, ndi pa okwera pa akavalo ace.

19. Ndipo mthenga wa Mulungu, wakutsogolera ulendo wa Israyeli, unacokako, nutsata pambuyo pao; ndipo mtambo njo uja unacoka patsogolo pao, nuima pambuyo pao;

20. nulowa pakati pa ulendo wa Aaigupto ndi ulendo wa Aisrayeli ndipo mtambo unacita mdima, komanso unaunikira usiku; ndipo ulendo wina sunayandikizana ndi unzace usiku wonse.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 14