20. Koma Yehova analimbitsa mtima wa Farao, ndipo sanalola ana a Israyeli amuke.
21. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tambasulira dzanja lako kuthambo, ndipo padzakhala mdima pa dziko la Aigupto, ndiwo mdima wokhudzika.
22. Ndipo Mose anatambasulira dzanja lace kuthambo; ndipo munali mdima bii m'dziko lonse la Aigupto masiku atatu;
23. sanaonana, sanaukanso munthu pamalo pace, masiku atatu; koma kwa ana onse a Israyeli kudayera m'nyumba zao.
24. Ndipo Farao anaitana Mose, nati, Mukani, tumikirani Yehova; nkhosa zanu ndi ng'ombe zanu zokha zitsale; mumuke nao ana anu ang'ononso.
25. Koma Mose anati, Mutipatsenso m'dzanja mwathu nsembe zophera ndi nsembe zopsereza, kuti timkonzere Yehova Mulungu wathu.