Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 10:18-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo anaturuka kwa Farao, napemba Yehova.

19. Ndipo Yehova anabweza mphepo yolimbatu ya kumadzulo, imene inapita nalo dzombe niliponya m'Nyanja Yofiira: silinatsala dzombe limodzi pakati pa malire onse a Aigupto.

20. Koma Yehova analimbitsa mtima wa Farao, ndipo sanalola ana a Israyeli amuke.

21. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tambasulira dzanja lako kuthambo, ndipo padzakhala mdima pa dziko la Aigupto, ndiwo mdima wokhudzika.

22. Ndipo Mose anatambasulira dzanja lace kuthambo; ndipo munali mdima bii m'dziko lonse la Aigupto masiku atatu;

23. sanaonana, sanaukanso munthu pamalo pace, masiku atatu; koma kwa ana onse a Israyeli kudayera m'nyumba zao.

24. Ndipo Farao anaitana Mose, nati, Mukani, tumikirani Yehova; nkhosa zanu ndi ng'ombe zanu zokha zitsale; mumuke nao ana anu ang'ononso.

25. Koma Mose anati, Mutipatsenso m'dzanja mwathu nsembe zophera ndi nsembe zopsereza, kuti timkonzere Yehova Mulungu wathu.

26. Zoweta zathu zomwe tidzapita nazo; cosatsala ciboda cimodzi; pakuti mwa izo tiyenera kutenga zakutumikira nazo Yehova Mulungu wathu; ndipo tisanafikeko, sitidziwa umo tidzamtumikira Yehova.

27. Koma Yehova analimbitsa mtima wace wa Farao, ndipo anakana kuwaleka amuke.

28. Ndipo Farao ananena naye, Coka pano, uzicenjera usaonenso nkhope yanga; pakuti tsiku limene uonanso nkhope yanga udzafa.

29. Ndipo Mose anati, Mwanena bwino; sindidzaonanso nkhope yanu.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 10