Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 9:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo ndinapemphera kwa Yehova ndi kuti, Yehova Mulungu, musaononga anthu anu ndi colowa canu, amene mudawaombola mwa ukulu wanu, amene munawaturutsa m'Aigupto ndi dzanja lamphamvu,

27. Kumbukilani atumiki anu, Abrahamu, Isake, ndi Yakobo; musapenyerera kupulukira kwa anthu awa, kapena coipa cao, kapena cimo lao;

28. kuti linganene dziko limene mudatiturutsako, Popeza Yehova sanakhoza kuwalowetsa m'dziko limene adanena nao, ndi popeza anadana nao, anawaturutsa kuti awaphe m'cipululu.

29. Koma iwo ndiwo anthu anu ndi colowa canu, amene mudaturutsa ndi mphamvu yanu yaikuru ndi dzanja lanu lotambasuka.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 9