Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 7:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene Yehova Mulungu wanu atakulowetsani m'dziko limene mumkako kulilandira likhale lanu lanu, ndipo atakataya amitundu ambiri pamaso panu, Ahiti, ndi Agirigazi, ndi Aamori, ndi Akanani, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi, mitundu isanu ndi iwiri yaikuru ndi yamphamvu yoposa inu;

2. nakawapereka Yehova Mulungu wanu pamaso panu, ndipo mukawakanthe; pamenepo muwaononge konse; musapangana nao pangano, kapena kuwacitira cifundo.

3. Ndipo musakwatitsane nao; musampatsemwana wace wamwamuna mwana wanu wamkazi, kapena kutenga mwana wace wamkazi akhale wa mwana wanu wamwamuna.

4. Popeza adzapatutsa mwana wanu aleke kunditsata Ine, kuti atumikire milungu yina; potero Yehova adzapsa mtima pa inu, ndipo adzakuonongani msanga.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 7