Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 5:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Usaphe.

18. Usacite cigololo.

19. Usabe.

20. Usamnamizire mnzako.

21. Usasirire mkazi wace wa mnzako; usakhumbe nyumba yace ya mnzako, munda wace, kapena wanchito wace wamwamuna, kapena wanchito wace wamkazi, ng'ombe yace, kapena buru wace, kapena kanthu kali konse ka mnzako.

22. Yehova ananena mau awa kwa msonkhano wanu wonse, m'phirimo ali pakati pa moto, pamtambo, pamdima bii, ndi mau akuru; osaonjezapo kanthu. Ndipo anawalembera pa magome awiri amiyala, nandipatsa awa.

23. Ndipo kunali, pamene munamva liu loturuka pakati pa mdima, potentha phiri ndi moto, munayandikiza kwa ine, ndiwo mafumu onse a mapfuko anu ndi akuru anu;

24. ndipo munati, Taonani, Yehova Mulungu wathu anationetsa ulemerero wace, ndi ukuru wace, ndipo tidamva liu lace ali pakati pa mote; tapenya lero lino kuti Mulungu anena ndi munthu, ndipo akhala ndi moyo.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 5