Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 3:3-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Potero Yehova Mulungu wathu anaperekanso m'manja mwathu Ogi mfumu ya Basana, ndi anthu ace onse, ndipo tinamkantha kufikira sanamtsalira ndi mmodzi yense.

4. Ndipo muja tinalanda midzi yace yonse; kunalibe mudzi sitinaulanda m'manja mwao, midzi makumi asanu ndi limodzi, dera lonse la Arigobi, dziko la Ogi m'Basana.

5. Yonseyi ndiyo midzi yozinga ndi malinga atali, zitseko, ndi mipiringidzo; pamodzi ndi midzi yambirimbiri yopanda malinga.

6. Ndipo tinaiononga konse, monga umo tinacitira Sihoni mfumu ya Hesiboni, ndi kuononga konse midzi yonse, amuna, akazi ndi ana.

7. Koma zoweta zonse ndi zofunkha za m'midzi, tinadzifunkhira tokha.

8. Ndipo muja tinalanda dziko m'manja mwa mafumu awiri a Aamori okhala tsidya lija la Yordano, kuyambira mtsinje wa Arinoni kufikira phiri la Herimoni;

9. (Asidoni alicha Herimoni Sirioni, koma Aamori alicha Seniri);

10. midzi yonse ya kucidikha, ndi Gileadi lonse, ndi Basana lonse kufikira ku Saleka ndi Edrei, midzi ya dziko la Ogi m'Basana.

11. (Pakuti Ogi mfumu ya Basana anatsala yekha wa iwo otsalira Arefai; taonani, kama wace ndiye kama wacitsulo; sukhala kodi m'Raba wa ana a Amoni? utali wace mikono isanu ndi inai, kupingasa kwace mikono inai, kuyesa mkono wa munthu.)

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 3