Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 3:18-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo ndinauza inu muja, ndi kuti, Yehova Mulungu wanu wakupatsani dziko ili likhale lanu lanu, muoloke, amuna onse amphamvu obvala zida zao, pamaso pa abale anu ana a Israyeli.

19. Koma akazi anu, ndi ana anu, ndi zoweta zanu, (ndidziwa muli nazo zoweta zambiri), zikhale m'midzi yanu imene ndinakupatsani;

20. kufikira Yehova atapumulitsa abale anu, monga anapumulitsa inu, nalandira iwonso dziko limene Yehova Mulungu wanu awapatsa tsidya lila la Yordano; pamenepo mudzabwerera munthu yense ku colowa cace, cimene ndinakupatsani.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 3