Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 29:1-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Awa ndi mau a cipangano cimene Yehova analamulira Mose acicite ndi ana a Israyeli m'dziko la Moabu, pamodzi ndi cipanganoco anacita nao m'Horebe.

2. Ndipo Mose anaitana Israyeli wonse, nati nao, Munapenya inu zonse zimene Yehova anacitira Farao, ndi anyamata ace onse, ndi dziko lace lonse, pamaso panu m'dziko la Aigupto;

3. mayesero akuruwa maso anu anawapenya, zizindikilozo, ndi zozizwa zazikuru zija;

4. koma Yehova sanakupatsani mtima wakudziwa, ndi maso akupenya, ndi makutu akumva, kufikira lero lino.

5. Ndipo ndinakutsogolerani zaka makumi anai m'cipululu; zobvala zanu sizinatha pathupi panu, ndi nsapato zanu sizinatha pa phazi lanu.

6. Simunadya mkate, simunamwa vinyo kapena cakumwa colimba; kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

7. Ndipo pamene munafika pamalo pano, Sihoni mfumu ya Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya Basana, anaturuka kudzakomana nafe kunkhondo, ndipo tinawakantha;

8. ndipo tinalanda dziko lao, ndi kulipereka likhale colowa cao ca Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la hafu la Manase.

9. Cifukwa cace sungani mau a cipangano ici ndi kuwacita, kuti mucite mwanzeru m'zonse muzicita.

10. Muimirira inu nonse lero lino pamaso pa Yehova Mulungu wanu; mafumu anu, mapfuko anu, akuru anu, ndi akapitao anu, amuna onse a Israyeli;

11. makanda anu, akazi anu, ndi mlendo wanu wakukhala pakati pa zigono zanu, kuyambira wotema nkhuni kufikira wotunga madzi;

12. kuti mulowe cipangano ca Yehova Mulungu wanu, ndi lumbiriro lace, limene Yehova Mulungu wanu acita ndi inu lero lino;

13. kuti adzikhazikire inu, mtundu wace wa anthu lero lino, ndi kuti akhale kwa inu Mulungu, monga ananena ndi inu, ndi monga analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isake, ndi Yakobo.

14. Koma sindicita cipangano ici ndi lumbiro ili ndi inu nokha;

15. komanso ndi iye wakuimirira pano nafe lero lino pamaso pa Yehova Mulungu wathu, ndiponso ndi iye wosakhala pano nafe lero lino.

16. Pakuti mudziwa cikhalidwe cathu m'dziko la Aigupto, ndi kuti tinapyola pakati pa amitundu amene munawapyola;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 29