Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 28:41-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Mudzabala ana amuna ndi akazi, osakhala nao, popeza adzalowa ukapolo.

42. Mitengo yanu yonse ndi zipatso za nthaka yanu zidzakhala zao zao za dzombe.

43. Mlendo wokhala pakati panu adzakulira-kulira inu, koma inu mudzacepera-cepera.

44. Iye adzakukongoletsani, osamkongoletsa ndinu; iye adzakhala mutu, koma inu ndinu mcira.

45. Ndipo matemberero awa onse adzakugwerani, nadzakulondolani, ndi kukupezani, kufikira mwaonongeka, popeza simunamvera mau a Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ace ndi malemba ace amene anakulamulirani;

46. ndipo zidzakukhalirani inu ndi mbeu zanu ngati cizindikilo ndi cozizwa, nthawi zonse.

47. Popeza simunatumikira Yehova Mulungu wanu ndi cimwemwe ndi mokondwera mtima, cifukwa ca kucuruka zinthu zonse;

48. cifukwa cace mudzatumikira adani anu amene Yehova adzakutumizirani, ndi njala, ndi ludzu, ndi usiwa, ndi kusowa zinthu zonse; ndipo adzaika goli lacitsulo pakhosi panu, kufikira atakuonongani.

49. Yehova adzakutengerani mtundu wa anthu wocokera kutali ku malekezero a dziko lapansi, monga iuluka mphungu; mtundu wa anthu amene simunamva malankhulidwe ao;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 28