Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 28:13-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo Yehova adzakuyesani mutu, si mcira ai; ndipo mudzakhala wa pamwamba pokha, si wapansi ai; ngati mudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu, amene ndikuuzani lero, kuwasunga ndi kuwacita;

14. osapatukira mau ali onse ndikuuzani lero, kulamanja, kapena kulamanzere, kutsata milungu yina kuitumikira.

15. Koma kudzali, mukapanda kumvera mau a Yehova Mulungu wanu, kusamalira kucita malamulo ace onse ndi malemba ace amene ndikuuzani lero, kuti matemberero awa onse adzakugwerani ndi kukupezani,

16. Mudzakhala otembereredwa m'mudzi, ndi otembereredwa pabwalo.

17. Zidzakhala zotembereredwa mtanga wanu ndi coumbiramo mkate wanu.

18. Zidzakhala zotembereredwa zipatso za thupi lanu, ndi zipatso za nthaka yanu, zoswana za ng'ombe zanu, ndi zoswana za nkhosa zanu.

19. Mudzakhala otembereredwa polowa inu, ndi otembereredwa poturuka inu.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 28