Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 24:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Musamasautsa wolembedwa nchito, wakukhala waumphawi ndi wosauka, wa abale anu kapena wa alendo ali m'dziko mwanu, m'midzi mwanu.

15. Pa tsiku lace muzimpatsa kulipira kwace, lisalowepo dzuwa; pakuti ndiye waumphawi, ndi mtima wace ukhumba uku; kuti angakulirireni kwa Yehova, ndipo kukukhaireni cimo.

16. Atate asaphedwere ana, ndi ana asaphedwere atate; munthu yense aphedwere cimo lace lace.

17. Musamaipsa mlandu wa mlendo, kapena wa ana amasiye; kapena kutenga cikole cobvala ca mkazi wamasiye;

18. koma muzikumbukila kuti munali akapolo m'Aigupto, ndi kuti Yehova Mulungu wanu anakuombolaniko; cifukwa cace ndikuuzani kucita cinthu ici.

19. Mutasenga dzinthuzanu m'munda mwanu, ndipo mwaiwala mtolo m'mundamo, musabwererako kuutenga; ukhale wa mlendo, wa mwana wamasiye, ndi wa mkazi wamasiye; kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni m'nchito zonse za manja anu.

20. Mutagwedeza mtengo wanu wa azitona musayesenso nthambi mutatha nazo; akhale a mlendo, a mwana wamasiye, ndi a mkazi wamasiye.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 24