1. Munthu wophwetekwa, wophwanyika kapena wofulika, asalowe m'msonkhano wa Yehova.
2. Mwana wa m'cigololo asalowe m'msonkhano wa Yehova, ngakhale mbadwo wace wakhumi usalowe m'msonkhano wa Yehova.
3. M-amoni kapena Mmoabu asalowe m'msonkhano wa Yehova; ngakhale mbadwo wao wakhumi usalowe m'msonkhano wa Yehova, ku nthawi zonse;
4. popeza sanakukumikani ndi mkate ndi madzi m'njira muja munaturuka m'Aigupto; popezanso anakulembererani Balamu mwana wa Beori wa ku Petori wa Mesapotamiya, kuti akutemberereni.
5. Ndipo Yehova Mulungu wanu sanafuna kumvera Balamu; koma Yehova Mulungu wanu anakusandulizirani tembererolo likhale mdalitso, popeza Yehova Mulungu wanu anakukondani.
6. Musawafunira mtendere, kapena cowakomera masiku anu onse ku nthawi zonse.
7. Musamanyansidwa naye M-edomu, popeza ndiye mbale wanu; musamanyansidwa naye M-aigupto, popeza munali alendo m'dziko lace.
8. Ana obadwa nao a mbadwo wacitatu alowe m'msonkhano wa Yehova.
9. Nkhondo yanu ikaturuka pa adani anu, mudzisunge kusacita coipa ciri conse.