Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 21:5-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. ndipo ansembe, ana a Levi, ayandikize; pakuti Yehova Mulungu wanu anasankha iwo kumtumikira ndi kudalitsa m'dzina la Yehova; ndipo kutengana konse ndi kupandana konse kukonzeke monga mwa mau awa.

6. Ndipo akuru onse a mudziwo wokhala pafupi pa munthu wophedwayo azisamba manja ao pa msoti woudula khosi m'cigwamo;

7. nayankhe nati, Manja athu sanakhetsa mwazi uwu, ndi maso athu sanauona.

8. Landirani, Yehova, cotetezera anthu anu Israyeli, amene munawaombola, ndipo musalole mwazi wosacimwa ukhale pakati pa anthu anu Israyeli; ndipo adzawatetezera ca mwaziwo.

9. Cotero mudzicotsere mwazi wosacimwa pakati panu, pakuti wacita coyenera pamaso pa Yehova.

10. Pamene muturuka kumka ku nkhondo ya pa adani anu, ndipo Yehova Mulungu wanu awapereka m'manja mwanu, ndipo muwagwira akhale akapolo anu;

11. mukaona mwa akapolowa mkazi wokongola, mukamkhumba, ndi kufuna kumtenga akhale mkazi wanu;

12. pamenepo mufike naye kwanu ku nyumba yanu; ndipo amete tsitsi la pamutu pace, ndi kuwenga makadabo ace;

13. nabvule zobvala za ukapolo wace, nakhale m'nyumba mwanu, nalire atate wace, ndi mai wace mwezi wamphumphu; ndipo atatero mulowe naye ndi kukhala mwamuna wace, ndi iye akhale mkazi wanu.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 21