Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 21:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Akapeza munthu waphedwa m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu lanu, nagona pamunda, wosadziwika wakumkantha,

2. pamenepo azituruka akuru anu ndi oweruza anu, nayese ku midzi yomzinga wophedwayo;

3. ndipo kudzali kuti mudzi wakukhala kufupi kwa munthu wophedwayo, inde akuru a mudzi uwu atenge ng'ombe yamsoti yosagwira nchito, yosakoka goli;

4. ndipo akuru a mudzi uwu atsike nao msotiwo ku cigwa coyendako madzi, cosalima ndi cosabzala, naudula khosi msotiwo m'cigwamo;

5. ndipo ansembe, ana a Levi, ayandikize; pakuti Yehova Mulungu wanu anasankha iwo kumtumikira ndi kudalitsa m'dzina la Yehova; ndipo kutengana konse ndi kupandana konse kukonzeke monga mwa mau awa.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 21