Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 15:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. cokhaci mumvere cimverere mau a Yehova Mulungu wanu, kuti musamalire kucita malamulo awa onse amene ndikuuzani lero lino.

6. Popeza Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani, monza ananena nanu; ndipo mudzakongoletsa amitundu ambiri, osakongola nokha; nimudzacita ufumu pa amitundu ambiri, koma iwo sadzacita ufumu pa inu.

7. Akakhala ndi inu munthu waumphawi, ndiye wilia wa abale anu, m'umodzi wa midzi yanu, m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, musakhakala mtima wanu, kapena kuumitsa dzanja lanu kukaniza mbale wanu waumphawi;

8. koma muzimtansira dzanjalanundithu ndi kumkongoletsa ndithu zofikira kusowa kwace, monga umo amasowa.

9. Dzicenjerani, mungakhale mau opanda pace mumtima mwanu, ndi kuti, Cayandika caka cacisanu ndi ciwiri, caka ca cilekerero; ndipo diso lanu lingaipire mbale wanu waumphawi, osampatsa kanthu; ndipo iye angalirire inu kwa Yehova; ndipo mwa inu mungakhale cimo.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 15