Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 11:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Potero muzisunga malamulo onsewa ndikuuzani lero lino, kuti mukhale amphamvu, ndi kulowa ndi kulandira dziko, limene mumkako kulilandira;

9. ndi kuti masiku anu acuruke m'dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, kuti adzawapatsa iwo ndi mbeu zao, dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

10. Pakuti dziko limene mumkako kulilandira ndi losanga dziko la Aigupto lija mudaturukako, kumene kuja munafesa mbeu zanu, ndi kuzithirira ndi phazi lanu, monga munda watherere;

11. koma dziko limene mumkako kulilandira ndilo dziko la mapiri ndi zigwa; limamwa madzi a mvula ya kumwamba;

12. ndilo dziko loti Yehova Mulungu wanu alisamalira, maso a Yehova Mulungu wanu akhalapo cikhalire, kuyambira caka mpaka kutsiriza caka.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 11