Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 10:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo ndinatembenuka ndi kutsika m'phiri, ndi kuika magome m'likasa ndinalipanga, ali m'menemo monga Yehova anandilamulira ine.

6. Ndipo ana a Israyeli anayenda ulendo wao kucokera ku zitsime za ana a Yaakani kufikira ku Mosera. Kumeneko anamwalira Aroni, ndi kumeneko anamuika; ndipo Eleazara mwana wace anacita nchito ya nsembe m'malo mwace.

7. Kucokerako anamka ulendo ku Gudigoda, ndi kucokera ku Gudigoda kumka ku Yotibata, dziko la mitsinje yamadzi.

8. Masiku aja Yehova anapatula pfuko la Levi, linyamule likasa la cipangano la Yehova, liimirire pamaso pa Yehova kumtumikira, ndi kudalitsa m'dzina lace kufikira lero lino.

9. Cifukwa cace Levi alibe gawo kapena colowa pamodzi ndi abale ace; Yehova mwini wace ndiye colowa cace, monga Yehova Mulungu wace ananena naye.

10. Ndipo ndinakhala m'phiri monga poyamba paja, masiku makumi anai usana ndi usiku; ndipo Yehova anandimvera ine pameneponso; Yehova sanafuna kukuonongani.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 10