Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 10:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo analembera pamagome, monga mwa malembedwe oyamba, mau khumiwo, amene Yehova adanena ndi inu m'phirimo, ali pakati pa moto, tsiku la kusonkhanako; ndipo Yehova anandipatsa awa.

5. Ndipo ndinatembenuka ndi kutsika m'phiri, ndi kuika magome m'likasa ndinalipanga, ali m'menemo monga Yehova anandilamulira ine.

6. Ndipo ana a Israyeli anayenda ulendo wao kucokera ku zitsime za ana a Yaakani kufikira ku Mosera. Kumeneko anamwalira Aroni, ndi kumeneko anamuika; ndipo Eleazara mwana wace anacita nchito ya nsembe m'malo mwace.

7. Kucokerako anamka ulendo ku Gudigoda, ndi kucokera ku Gudigoda kumka ku Yotibata, dziko la mitsinje yamadzi.

8. Masiku aja Yehova anapatula pfuko la Levi, linyamule likasa la cipangano la Yehova, liimirire pamaso pa Yehova kumtumikira, ndi kudalitsa m'dzina lace kufikira lero lino.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 10