Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 1:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo kunali, caka ca makumi anai, mwezi wakhumi ndi umodzi, tsiku loyamba la mweziwo, Mose ananena ndi ana a Israyeli, monga mwa zonse Yehova adamlamulira awauze;

4. atakantha Sihoni mfumu ya Aamori, wakukhala m'Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya Basana, wakukhala m'Asitaroti, ku Edrei.

5. Tsidya lija la Yordano, m'dziko la Moabu, Mose anayamba kufotokozera cilamulo ici, ndi kuti.

6. Yehova Mulungu wathu ananena ndi ife m'Horebe, ndi kuti, Yakwanira nthawi yokhala inu m'phiri muno;

7. bwererani, yendani ulendo wanu ndi kumuka ku mapiri a Aamori, ndi koyandikizana nao, kucidikha, kumapiri, ndi kunsi ndi kumwela, ndi kumphepete kwa nyanja, dziko la Akanani, ndi Lebano, kufikira nyanja yaikuru Firate.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 1